Amangidwa atapezeka ndi Chamba.

Wolemba William Chitengu Jnr

A Polisi m’boma la Salima amanga abambo atatu kamba kopezeka ndi chamba opanda chilorezo.

Malingana ndi Mneneri wa polisi ya Salima, Sub inspector Rabecca ndiwate abambo atatuwa agwidwa usiku wapa 25/26 April 2025 pamene apolisi anaika malo ochitira chipikisheni pafupi ndi malo omwetsera mafuta a mlamba mseu wa Salima-Balaka.

Oganiziridwa oyamba a Mickson Thomson azaka 37, awanga potsatira a polisi kufufuza galimoto yomwe amayendera ndipo anapeza thumba lomwe munali chambachi.

A Mathews Mafuta a zaka 40, komanso a Happy Chiumia a zaka 27, amangidwa pamene amafuna kuzembetsa chambachi pogwiritsa ntchito njinga za moto.

Atatuwa akaonekera ku bwalo la milandu posachedwapa pamene akayankhe milandu yokhudza nkhaniyi.

Related posts

Lost Glimmer of Hope: Farmers Await a Market That Never Came.

Plane Crash Inquiry making progress.

Anthu apemphedwa kutsatira njira zopewera zibayo.

2 comments

Jerry300 April 27, 2025 - 1:40 am
Very good https://t.ly/tndaA
Janet2140 April 27, 2025 - 10:20 am
Very good https://t.ly/tndaA
Add Comment