Amangidwa atapezeka ndi Chamba.

Wolemba William Chitengu Jnr

A Polisi m’boma la Salima amanga abambo atatu kamba kopezeka ndi chamba opanda chilorezo.

Malingana ndi Mneneri wa polisi ya Salima, Sub inspector Rabecca ndiwate abambo atatuwa agwidwa usiku wapa 25/26 April 2025 pamene apolisi anaika malo ochitira chipikisheni pafupi ndi malo omwetsera mafuta a mlamba mseu wa Salima-Balaka.

Oganiziridwa oyamba a Mickson Thomson azaka 37, awanga potsatira a polisi kufufuza galimoto yomwe amayendera ndipo anapeza thumba lomwe munali chambachi.

A Mathews Mafuta a zaka 40, komanso a Happy Chiumia a zaka 27, amangidwa pamene amafuna kuzembetsa chambachi pogwiritsa ntchito njinga za moto.

Atatuwa akaonekera ku bwalo la milandu posachedwapa pamene akayankhe milandu yokhudza nkhaniyi.

Related posts

Salima District joins global GBV commemoration.

‘Adopt the Needy Students’ Initiative Unveiled at UNIMA Alumni AGM.

10 Years imprisonment for breaking a house.

2 comments

Jerry300 April 27, 2025 - 1:40 am
Very good https://t.ly/tndaA
Janet2140 April 27, 2025 - 10:20 am
Very good https://t.ly/tndaA
Add Comment