SADFA ili ndi adindo atsopano.

Chithunzi Adams Cuba Phiri.

Wolemba Liana Bonongwe

Adams Curba Phiri ndiye wapambana pa udindo wa wapampando wa Salima district football association (SADFA) atagonjetsa yemwe anali wapampando wabungweri Abdul Salaam Mtimbwinda ndi ma vote 33 kwa 9.

Chisankhochi chachitika loweluka ku Matenje Teachers Development Center (TDC) pomwe nthumwi zotsatira masewero a Mpira kuchokera muma zone onse a m’boma anaponya vote.

Sheikh Ibrahim Omar ndi amene apambana pa udindo wa wachiwiri kwa wapampando opanda opikisana naye.

Mu mkuyankhula kwake atapambana Phiri wati agwira ntchito ndi aliyese pofuna kupititsa patsogolo mpira m’boma la Salima.

Iye wati ali ndi masomphenya obweletsa team ya Nyasa Big bullets kuzakumana ndi team yochokera m’boma la Salima pamene Bwalo la zamasewero la Community lizidzatsegulidwa.

Related posts

Salima District joins global GBV commemoration.

‘Adopt the Needy Students’ Initiative Unveiled at UNIMA Alumni AGM.

10 Years imprisonment for breaking a house.