Kutsimikiza mayina kwayamba bwino

Wolemba Stella Chasowa

Komishonala wa Bungwe la MEC Emmanuel Fabiano wati ndiokhutira ndi momwe ntchito yotsimikiza mayina mukaundula wa voti yayambira m’boma la Salima

Iye wayankhula izi lachiwiri atayendera malo amene kukuchitika ntchito yotsimikiza mainayi m’bomali

Fabiano anati malo omwe iye wayendera chilichonse chikuyenda bwino ndipo sanalandireko dandaulo lililonse.

“Pakadali pano mmalo omwe ndapitapo palibe pomwe ndauzidwa kuti panali dandaulo kapena vuto lina lilonse kwa anthu omwe akudzatsimikiza maina awo” fabiyano watero

Iye anapitiriza kumema atsogoleri azipani kuti atumize nthumwi zawo pa malo omwe pakichitikira ntchitoyi.

Gawo loyamba lotsimikiza maina mu kaundula wa mavoti layamba lachiwiri pa 13 May ndipo litha pa 15 May 2025.

Related posts

Salima District joins global GBV commemoration.

‘Adopt the Needy Students’ Initiative Unveiled at UNIMA Alumni AGM.

10 Years imprisonment for breaking a house.